AONESA CHIDWI CHODZAPIKISANA NAWO NGATI KHASALA

 

Modzi mwa achinyamata okhala pa Nathenje  Gift Mkochi watsimikiza kuti ayimira nawo ngati Khasala wa Ngala Ward pachisankho chomwe chichitike chaka cha mawa dziko muno.

a Mkochi ati akufuna kudzapikisana nawo pa chisankhochi atawona kuti kwanthawi yayitali Ngala Ward yatsalira Ku nkhani ya chitukuko. 

"Inetu ndi mwana wamudzi muno, ndaphunzira konkuno ndipo zanga zonse zili kuno. Ndi zokhumudwitsa kuti ntchito ya Khasala kwathu kuno sikudziwika!!! Ndikufuna anthu adziwe kuti Khasala amatani" anayakhula motero a Mkochi

Iwoso atsimikiza kuti akonzeka kukathamangitsana ndi anzawo ena kumasankho achipulura a chipani cha Malawi Kongelesi mwezi wa seputembala uno

Wolemba: Alinafe Jonasi & Loveness Chiutsi

Chithunzi: Shadow Khasala Gift Mkochi



Comments

Popular posts from this blog

AFTER DEADLY PROTESTS, KENYANS TELL OF BRUTAL ABDUCTIONS

TIDIKIRE MPAKA AYAKE - CHIFUKWA IZI NDIYE NDI KHWESI